5
Wolamulira Wochokera ku Betelehemu
Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo,
pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe.
Adzakantha ndi ndodo pa chibwano
cha wolamulira wa Israeli.
 
“Koma iwe Betelehemu Efurata,
ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda,
mwa iwe mudzatuluka
munthu amene adzalamulira Israeli,
amene chiyambi chake nʼchakalekale,
nʼchamasiku amakedzana.”
 
Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa
mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire.
Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera
kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
 
Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake
mwa mphamvu ya Yehova,
mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake.
Ndipo iwo adzakhala mu mtendere,
pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo.
Chipulumutso ndi Chiwonongeko
Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu
ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa,
tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri,
ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga,
dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo.
Adzatipulumutsa kwa Asiriya
akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu
kudzatithira nkhondo.
 
Otsalira a Yakobo adzakhala
pakati pa mitundu yambiri ya anthu
ngati mame ochokera kwa Yehova,
ngati mvumbi pa udzu,
omwe sulamulidwa ndi munthu
kapena kudikira lamulo la anthu.
Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu,
mʼgulu la anthu a mitundu yambiri,
ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango.
Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa,
amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula,
ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
Mudzagonjetsa adani anu,
ndipo adani anu onse adzawonongeka.
10 Yehova akuti,
“Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse
ndi kuphwasula magaleta anu.
11 Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu
ndi kugwetsa malinga anu onse.
12 Ndidzawononga ufiti wanu
ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
13 Ndidzawononga mafano anu osema
pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu;
simudzagwadiranso zinthu zopanga
ndi manja anu.
14 Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu,
ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
15 Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya
mitundu imene sinandimvere Ine.”