Salimo 101
Salimo la Davide.
Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama;
kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.
Ndidzatsata njira yolungama;
nanga mudzabwera liti kwa ine?
 
Ndidzayenda mʼnyumba mwanga
ndi mtima wosalakwa.
Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa
pamaso panga.
 
Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro;
iwo sadzadziphatika kwa ine.
Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine;
ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.
 
Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri
ameneyo ndidzamuletsa;
aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza,
ameneyo sindidzamulekerera.
 
Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko,
kuti akhale pamodzi ndi ine;
iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa
adzanditumikira.
 
Aliyense wochita chinyengo
sadzakhala mʼnyumba mwanga.
Aliyense woyankhula mwachinyengo
sadzayima pamaso panga.
 
Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu
onse oyipa mʼdziko;
ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa
mu mzinda wa Yehova.