Salimo 121
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
Ndikweza maso anga ku mapiri;
kodi thandizo langa limachokera kuti?
Thandizo langa limachokera kwa Yehova,
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
 
Sadzalola kuti phazi lako literereke;
Iye amene amakusunga sadzawodzera.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli
sadzawodzera kapena kugona.
 
Yehova ndiye amene amakusunga;
Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,
kapena mwezi nthawi ya usiku.
 
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;
adzasunga moyo wako.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;
kuyambira tsopano mpaka muyaya.