Salimo 124
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
madzi a mkokomo
akanatikokolola.
 
Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.