Salimo 140
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;
tetezeni kwa anthu ankhanza,
amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa
ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;
pa milomo yawo pali ululu wa mamba.
Sela
 
Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;
tchinjirizeni kwa anthu ankhanza
amene amakonza zokola mapazi anga.
Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;
iwo atchera zingwe za maukonde awo
ndipo anditchera misampha pa njira yanga.
Sela
 
Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
Imvani kupempha kwanga Yehova.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,
mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;
musalole kuti zokonza zawo zitheke,
mwina iwo adzayamba kunyada.
Sela
 
Mitu ya amene andizungulira
iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
10 Makala amoto agwere pa iwo;
aponyedwe pa moto,
mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;
choyipa chilondole anthu ankhanza.
 
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,
ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,
ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.