Salimo 144
Salimo la Davide.
Atamandike Yehova Thanthwe langa,
amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;
zala zanga kumenya nkhondo.
Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,
linga langa ndi mpulumutsi wanga,
chishango changa mmene ine ndimathawiramo,
amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
 
Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,
mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
Munthu ali ngati mpweya;
masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
 
Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;
khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;
ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;
landitseni ndi kundipulumutsa,
ku madzi amphamvu,
mʼmanja mwa anthu achilendo,
amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,
amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
 
Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;
ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
10 kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,
amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
 
11 Landitseni ndi kundipulumutsa,
mʼmanja mwa anthu achilendo,
amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,
amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
 
12 Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo
adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,
ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala
zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
13 Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza
ndi zokolola za mtundu uliwonse.
Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda
pa mabusa athu.
14 Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.
Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,
sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,
mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
 
15 Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;
odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.