Salimo 34
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka.
Ndidzayamika Yehova nthawi zonse;
matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Moyo wanga udzanyadira Yehova;
anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine;
tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
 
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha;
anandilanditsa ku mantha anga onse.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira;
nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva;
Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye
ndi kuwalanditsa.
 
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino;
wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake,
pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala
koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
 
11 Bwerani ana anga, mundimvere;
ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake
ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 asunge lilime lake ku zoyipa
ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;
funafuna mtendere ndi kuwulondola.
 
15 Maso a Yehova ali pa olungama
ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa,
kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
 
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva;
Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima
ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
 
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri,
Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Iye amateteza mafupa ake onse,
palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
 
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa;
adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Yehova amawombola atumiki ake;
aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.