Salimo 56
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati.
Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri;
tsiku lonse akundithira nkhondo.
Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse,
ambiri akumenyana nane monyada.
 
Ndikachita mantha
ndimadalira Inu.
Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,
mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.
Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
 
Tsiku lonse amatembenuza mawu anga;
nthawi zonse amakonza zondivulaza.
Iwo amakambirana, amandibisalira,
amayangʼanitsitsa mayendedwe anga
ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
 
Musalole konse kuti athawe;
mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
Mulembe za kulira kwanga,
mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu.
Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
 
Adani anga adzabwerera mʼmbuyo
pamene ndidzalirira kwa Inu.
Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda,
mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha.
Kodi munthu angandichite chiyani?
 
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu;
ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa
ndi mapazi anga kuti ndingagwe,
kuti ndiyende pamaso pa Mulungu
mʼkuwala kwa moyo.