Salimo 79
Salimo la Asafu.
Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu;
ayipitsa Nyumba yanu yoyera,
asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu
kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya,
matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
Akhetsa magazi monga madzi
kuzungulira Yerusalemu yense,
ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu,
choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
 
Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya?
Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina
amene sakudziwani Inu,
pa maufumu
amene sayitana pa dzina lanu;
pakuti iwo ameza Yakobo
ndi kuwononga dziko lawo.
Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu
chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe,
pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
 
Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu;
tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu
chifukwa cha dzina lanu.
10 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti,
“Ali kuti Mulungu wawo?”
Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina
kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
11 Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu;
ndi mphamvu ya dzanja lanu
muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
 
12 Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri
kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
13 Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu,
tidzakutamandani kwamuyaya,
kuchokera mʼbado ndi mʼbado
tidzafotokoza za matamando anu.