Salimo 87
Salimo la Ana a Kora.
Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
Yehova amakonda zipata za Ziyoni
kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
Za ulemerero wako zimakambidwa,
Iwe mzinda wa Mulungu:
Sela
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni
pakati pa iwo amene amandidziwa.
Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,
ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”
 
Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,
“Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,
ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:
“Uyu anabadwira mʼZiyoni.”
Sela
Oyimba ndi ovina omwe adzati,
“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”