Yesaya
1
Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
Anthu Owukira
Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!
Pakuti Yehova wanena kuti,
“Ndinabala ana ndi kuwalera,
koma anawo andiwukira Ine.
Ngʼombe imadziwa mwini wake,
bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,
koma Israeli sadziwa,
anthu anga samvetsa konse.”
 
Haa, mtundu wochimwa,
anthu olemedwa ndi machimo,
obadwa kwa anthu ochita zoyipa,
ana odzipereka ku zoyipa!
Iwo asiya Yehova;
anyoza Woyerayo wa Israeli
ndipo afulatira Iyeyo.
 
Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?
Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?
Mutu wanu wonse uli ndi mabala,
mtima wanu wonse wafowokeratu.
Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu
palibe pabwino,
paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,
mabala ali magazi chuchuchu,
mabala ake ngosatsuka, ngosamanga
ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
 
Dziko lanu lasanduka bwinja,
mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;
minda yanu ikukololedwa ndi alendo
inu muli pomwepo,
dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha
ngati nsanja mʼmunda wampesa,
ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,
ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
Yehova Wamphamvuzonse akanapanda
kutisiyira opulumuka,
tikanawonongeka ngati Sodomu,
tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
 
10 Imvani mawu a Yehova,
inu olamulira Sodomu;
mverani lamulo la Mulungu wathu,
inu anthu a ku Gomora!
11 Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani
nsembe zanu zochuluka?”
“Zandikola nsembe zanu zopsereza
za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;
sindikusangalatsidwanso
ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
12 Ndani anakulamulirani kuti
mubwere nazo pamaso panga?
Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
13 Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!
Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.
Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,
kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
14 Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika
ndimadana nazo.
Zasanduka katundu wondilemera;
ndatopa kuzinyamula.
15 Mukamatambasula manja anu popemphera,
Ine sindidzakuyangʼanani;
ngakhale muchulukitse mapemphero anu,
sindidzakumverani.
Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
16 sambani, dziyeretseni.
Chotsani pamaso panu
ntchito zanu zoyipa!
Lekani kuchita zoyipa,
17 phunzirani kuchita zabwino!
Funafunani chilungamo,
thandizani oponderezedwa.
Tetezani ana amasiye,
muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
 
18 Yehova akuti,
“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.
Ngakhale machimo anu ali ofiira,
adzayera ngati thonje.
Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,
adzayera ngati ubweya wankhosa.
19 Ngati muli okonzeka kundimvera
mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
20 koma mukakana ndi kuwukira
mudzaphedwa ndi lupanga.”
Pakuti Yehova wayankhula.
 
21 Taonani momwe mzinda wokhulupirika
wasandukira wadama!
Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;
mu mzindamo munali chilungamo,
koma tsopano muli anthu opha anzawo!
22 Siliva wako wasanduka wachabechabe,
vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
23 Atsogoleri ako ndi owukira,
anthu ogwirizana ndi mbala;
onse amakonda ziphuphu
ndipo amathamangira mphatso.
Iwo sateteza ana amasiye;
ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
24 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,
Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,
“Haa, odana nane ndidzawatha,
ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
25 Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;
ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,
monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
26 Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,
aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.
Kenaka iweyo udzatchedwa
mzinda wolungama,
mzinda wokhulupirika.”
 
27 Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,
anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
28 Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,
ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
 
29 “Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu
imene inkakusangalatsani;
mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda
imene munayipatula.
30 Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,
mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
31 Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,
ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;
motero zonse zidzayakira limodzi,
popanda woti azimitse motowo.”