Nyimbo ya Solomoni
1
Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
 
Mkazi
Undipsompsone ndi milomo yako
chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino;
dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa.
Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire!
Mfumu indilowetse mʼchipinda chake.
Abwenzi
Ife timasangalala ndi kukondwera nawe,
tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo.
Mkazi
Amachita bwinotu potamanda iwe!
 
Ndine wakuda, komatu ndine wokongola,
inu akazi a ku Yerusalemu,
ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara,
ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda,
ndine wakuda chifukwa cha dzuwa.
Alongo anga anandikwiyira
ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa;
munda wangawanga sindinawusamalire.
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako
ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana.
Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere
pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Abwenzi
Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena,
ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa
ndipo udyetse ana ambuzi
pambali pa matenti a abusa.
Mwamuna
Iwe bwenzi langa,
uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo,
khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide
zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Mkazi
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera,
mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine,
kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira,
ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
Mwamuna
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi!
Ndithu, ndiwe chiphadzuwa,
maso ako ali ngati nkhunda.
Mkazi
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi!
Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri!
Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Mwamuna
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza,
phaso lake ndi la mtengo wa payini.