Salimo 129
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”
anene tsono Israeli;
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,
koma sanandipambane.
Anthu otipula analima pa msana panga
ndipo anapangapo mizere yayitali:
Koma Yehova ndi wolungama;
Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
 
Onse amene amadana ndi Ziyoni
abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,
umene umafota usanakule;
sungadzaze manja a owumweta
kapena manja a omanga mitolo.
Odutsa pafupi asanene kuti,
“Dalitso la Yehova lili pa inu;
tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”