Salimo 130
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
Ndikulirira kwa Inu Yehova ndili mʼdzenje lozama;
Ambuye imvani mawu anga.
Makutu anu akhale tcheru kumva
kupempha chifundo kwanga.
 
Inu Yehova, mukanamawerengera machimo,
Inu Yehova, akanayima chilili ndani wopanda mlandu?
Koma kwa Inu kuli chikhululukiro;
nʼchifukwa chake mumaopedwa.
 
Ndimayembekezera Yehova, moyo wanga umayembekezera,
ndipo ndimakhulupirira mawu ake.
Moyo wanga umayembekezera Ambuye,
kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,
inde, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,
 
Yembekeza Yehova, iwe Israeli,
pakuti Yehova ali ndi chikondi chosasinthika
ndipo alinso ndi chipulumutso chochuluka.
Iye mwini adzawombola Israeli
ku machimo ake onse.